Yobu 29:1-25 OCCL

[1] Yobu anapitiriza kuyankhula kwake: [2] “Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira, [3] pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima! [4] Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga, [5] nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu, [6] pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi. [7] “Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo, [8] anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira; [9] atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo; [10] anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo. [11] Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira, [12] chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza. [13] Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye. [14] Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga. [15] Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala. [16] Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake. [17] Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa. [18] “Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga. [19] Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse. [20] Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’ [21] “Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga. [22] Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima. [23] Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe. [24] Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo. [25] Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.