[1] Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
[2] “Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
[3] pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
[4] Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
[5] nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
[6] pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
[7] “Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
[8] anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
[9] atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
[10] anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
[11] Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
[12] chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
[13] Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
[14] Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
[15] Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
[16] Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
[17] Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
[18] “Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
[19] Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
[20] Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
[21] “Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
[22] Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
[23] Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
[24] Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
[25] Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”