Yobu 28:1-28 OCCL
[1] Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide. [2] Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa. [3] Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani. [4] Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku. [5] Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto; [6] miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide. [7] Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona. [8] Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo. [9] Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde. [10] Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo. [11] Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika. [12] “Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti? [13] Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo. [14] Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’ [15] Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri. [16] Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro. [17] Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide. [18] Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi. [19] Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri. [20] “Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti? [21] Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga. [22] Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’ [23] Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala, [24] pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo. [25] Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja, [26] atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu, [27] pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe. [28] Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’ ”
