Yobu 30:1-31 OCCL
[1] “Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga. [2] Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale? [3] Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku. [4] Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache. [5] Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba. [6] Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka. [7] Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango. [8] Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko. [9] “Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo. [10] Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu. [11] Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa. [12] Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane. [13] Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa. [14] Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu. [15] Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo. [16] “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso. [17] Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka. [18] Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi. [19] Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa. [20] “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe. [21] Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu. [22] Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho. [23] Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako. [24] “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake. [25] Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka? [26] Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera. [27] Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso. [28] Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira. [29] Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi. [30] Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi. [31] Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.
