Yobu 20:1-29 OCCL
[1] Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti [2] “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri. [3] Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe. [4] “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi, [5] kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa. [6] Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa, [7] iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’ [8] Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku. [9] Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake. [10] Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka; [11] Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi. [12] “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake, [13] ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake, [14] koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo. [15] Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo. [16] Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha. [17] Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta. [18] Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake. [19] Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange. [20] “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho. [21] Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha. [22] Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera. [23] Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza. [24] Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa. [25] Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu; [26] mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake. [27] Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira. [28] Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu. [29] Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
