Yobu 19:1-29 OCCL
[1] Pamenepo Yobu anayankha kuti, [2] “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo? [3] Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi. [4] Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga. [5] Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane, [6] pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake. [7] “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama. [8] Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima. [9] Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga. [10] Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo. [11] Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake. [12] Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga. [13] “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine. [14] Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala. [15] Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo. [16] Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu. [17] Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi. [18] Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola. [19] Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira. [20] Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba. [21] “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha. [22] Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa? [23] “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku, [24] akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa! [25] Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza. [26] Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu. [27] Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi! [28] “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’ [29] Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
