Yobu 21:1-34 OCCL
[1] Pamenepo Yobu anayankha kuti, [2] “Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu. [3] Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze. [4] “Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima? [5] Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa. [6] Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera. [7] Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu? [8] Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona. [9] Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe. [10] Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza. [11] Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo. [12] Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro. [13] Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. [14] Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu. [15] Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo? [16] Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa. [17] “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga? [18] Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu? [19] Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi. [20] Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse. [21] Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha? [22] “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba? [23] Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo, [24] thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta. [25] Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse. [26] Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi. [27] “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire. [28] Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’ [29] Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena? [30] Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu? [31] Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita? [32] Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake. [33] Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho. [34] “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”
