Yobu 18:1-21 OCCL

[1] Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti, [2] “Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula. [3] Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako? [4] Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake? [5] “Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso. [6] Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima. [7] Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa. [8] Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo. [9] Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa. [10] Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake. [11] Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse. [12] Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira. [13] Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola. [14] Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse. [15] Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda. [16] Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota [17] Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko. [18] Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse. [19] Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala. [20] Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu. [21] Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.