[1] Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
[2] “Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
[3] Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
[4] Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
[5] “Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
[6] Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
[7] Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
[8] Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
[9] Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
[10] Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
[11] Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
[12] Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
[13] Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
[14] Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
[15] Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
[16] Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
[17] Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
[18] Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
[19] Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
[20] Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
[21] Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”