Miyambo 8:1-36 OCCL
[1] Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake? [2] Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu. [3] Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti, [4] Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse. [5] Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu. [6] Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama. [7] Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa. [8] Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka. [9] Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza. [10] Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino. [11] Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru. [12] Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino. [13] Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga. [14] Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu. [15] Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama. [16] Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko. [17] Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza. [18] Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika. [19] Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri. [20] Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo. [21] Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma. [22] “Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine. [23] Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe. [24] Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa. [25] Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale, [26] lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi. [27] Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama, [28] pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama, [29] pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi. [30] Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake. [31] Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.” [32] “Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga. [33] Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga. [34] Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa. [35] Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima. [36] Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”
