Miyambo 7:1-27 OCCL

[1] Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa. [2] Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako. [3] Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako. [4] Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.” [5] Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo. [6] Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera. [7] Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru. [8] Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo. [9] Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima. [10] Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga. [11] (Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo. [12] Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse). [13] Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti, [14] “Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga. [15] Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza! [16] Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto. [17] Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni. [18] Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi! [19] Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali: [20] Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.” [21] Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika. [22] Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha, [23] mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka. [24] Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena. [25] Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake. [26] Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu. [27] Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.