[1] Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
[2] Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
[3] Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
[4] “Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
[5] “Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
[6] Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
[7] Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
[8] Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
[9] Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
[10] Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
[11] Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
[12] Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
[13] Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
[14] Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
[15] kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
[16] Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
[17] “Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
[18] Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya.