Miyambo 9:1-18 OCCL

[1] Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri. [2] Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake. [3] Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti, [4] “Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti, [5] “Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza. [6] Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.” [7] Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake. [8] Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda. [9] Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake. [10] Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu. [11] Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa. [12] Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha. [13] Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu. [14] Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda, [15] kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo. [16] Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati, [17] “Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!” [18] Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.