Miyambo 6:1-35 OCCL
[1] Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo, [2] ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako. [3] Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule! [4] Usagone tulo, usawodzere. [5] Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka. [6] Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu! [7] Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira, [8] komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola. [9] Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti? [10] Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule, [11] umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba. [12] Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa, [13] amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake, [14] amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu. [15] Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa. [16] Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa: [17] maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa, [18] mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa, [19] mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale. [20] Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako. [21] Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako. [22] Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula. [23] Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni, [24] kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere. [25] Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake, [26] paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse. [27] Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa? [28] Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera? [29] Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa. [30] Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala. [31] Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake. [32] Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha. [33] Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera. [34] Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera. [35] Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.
