Miyambo 5:1-23 OCCL

[1] Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi, tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa, [2] kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo. [3] Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi. Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta, [4] koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu; ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse. [5] Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. [6] Iye saganizirapo za njira ya moyo; njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi. [7] Tsopano ana inu, mundimvere; musawasiye mawu anga. [8] Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo, usayandikire khomo la nyumba yake, [9] kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena; ndi zaka zako kwa anthu ankhanza, [10] kapenanso alendo angadyerere chuma chako ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena. [11] Potsiriza pa moyo wako udzabuwula, thupi lako lonse litatheratu. [12] Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo! Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo! [13] Sindinamvere aphunzitsi anga kapena alangizi anga. [14] Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke pakati pa msonkhano wonse.” [15] Imwa madzi a mʼchitsime chakochako, madzi abwino ochokera mʼchitsime chako. [16] Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu? Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda? [17] Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha, osati uyigawireko alendo. [18] Yehova adalitse kasupe wako, ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako. [19] Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino. Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse, ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse. [20] Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo? Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo? [21] Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona, ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse. [22] Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha; zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha. [23] Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo, adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.