[1] Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
[2] Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
[3] Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
[4] Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
[5] Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
[6] Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
[7] Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
[8] Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
[9] Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
[10] Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
[11] Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
[12] Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
[13] Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
[14] Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
[15] Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
[16] Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
[17] Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
[18] Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
[19] Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
[20] Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
[21] Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
[22] Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
[23] Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
[24] Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
[25] Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
[26] Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
[27] Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.