Miyambo 4:1-27 OCCL

[1] Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu. [2] Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga. [3] Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga. [4] Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo. [5] Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo. [6] Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza. [7] Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu. [8] Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu. [9] Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.” [10] Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka. [11] Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama. [12] Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa. [13] Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa. [14] Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa. [15] Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita. [16] Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina. [17] Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa. [18] Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu. [19] Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa. [20] Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga. [21] Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako. [22] Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse. [23] Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo. [24] Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa. [25] Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika. [26] Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa. [27] Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.