Miyambo 3:1-35 OCCL
[1] Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga. [2] Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere. [3] Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako. [4] Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu. [5] Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu. [6] Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako. [7] Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa. [8] Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba. [9] Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova. [10] Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo. [11] Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake. [12] Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye. [13] Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu, [14] pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide. [15] Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru. [16] Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu. [17] Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere. [18] Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri. [19] Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba. [20] Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula. [21] Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere. [22] Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi. [23] Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa; [24] pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma. [25] Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa, [26] pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha. [27] Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi. [28] Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano. [29] Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira. [30] Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa. [31] Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse. [32] Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama. [33] Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama. [34] Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa. [35] Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
