Miyambo 2:1-22 OCCL

[1] Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako, [2] ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu; [3] ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu, [4] ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika, [5] ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova. [6] Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu. [7] Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro, [8] pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika. [9] Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino. [10] Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa. [11] Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza. [12] Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza, [13] amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima, [14] amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa. [15] Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo. [16] Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika, [17] amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake. [18] Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda. [19] Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo. [20] Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo. [21] Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo; [22] Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.