Miyambo 22:1-29 OCCL

[1] Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide. [2] Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova. [3] Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo. [4] Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo. [5] Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo. [6] Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo. [7] Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo. [8] Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka. [9] Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka. [10] Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka. [11] Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu. [12] Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika. [13] Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!” [14] Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo. [15] Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo. [16] Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka. [17] Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe. [18] Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula. [19] Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova. [20] Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru, [21] malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo? [22] Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu, [23] pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo. [24] Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya [25] kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha. [26] Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole; [27] ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe. [28] Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako. [29] Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.