Miyambo 23:1-35 OCCL
[1] Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako, [2] ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo. [3] Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo. [4] Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa. [5] Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga. [6] Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma; [7] paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe. [8] Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe. [9] Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru. [10] Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye, [11] paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe. [12] Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso. [13] Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa. [14] Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. [15] Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera. [16] Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama. [17] Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku. [18] Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka. [19] Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino. [20] Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera. [21] Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza. [22] Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba. [23] Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino. [24] Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye. [25] Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere! [26] Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga. [27] Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza. [28] Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu. [29] Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira? [30] Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa. [31] Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino! [32] Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri. [33] Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera. [34] Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa. [35] Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”
