Miyambo 21:1-31 OCCL
[1] Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna. [2] Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake. [3] Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe. [4] Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa. [5] Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka. [6] Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa. [7] Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama. [8] Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama. [9] Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola. [10] Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika. [11] Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso. [12] Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo. [13] Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe. [14] Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa. [15] Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo. [16] Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa. [17] Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera. [18] Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima. [19] Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga. [20] Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga. [21] Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero. [22] Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira. [23] Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto. [24] Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri. [25] Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito. [26] Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja. [27] Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa! [28] Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse. [29] Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake. [30] Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova. [31] Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.
