Miyambo 1:1-33 OCCL
[1] Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli: [2] Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama; [3] kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera. [4] Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira. [5] Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso, [6] kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko. [7] Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo. [8] Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako. [9] Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako. [10] Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere. [11] Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa; [12] tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. [13] Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda; [14] Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.” [15] Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo. [16] Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi. [17] Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona! [18] Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha! [19] Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake. [20] Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika; [21] ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti, [22] “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti? [23] Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga. [24] Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala. [25] Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale. [26] Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho. [27] Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani. [28] “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza. [29] Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova, [30] popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa. [31] Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena. [32] Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo. [33] Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
