Masalimo 150:1-6 OCCL

[1] Tamandani Yehova. Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika; mutamandeni ku thambo lake lamphamvu. [2] Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu; mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana. [3] Mutamandeni poyimba malipenga, mutamandeni ndi pangwe ndi zeze. [4] Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina, mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro. [5] Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga, mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri. [6] Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova. Tamandani Yehova.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.