Masalimo 150:1-6 OCCL

[1] Tamandani Yehova. Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika; mutamandeni ku thambo lake lamphamvu. [2] Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu; mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana. [3] Mutamandeni poyimba malipenga, mutamandeni ndi pangwe ndi zeze. [4] Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina, mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro. [5] Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga, mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri. [6] Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova. Tamandani Yehova.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.