[1] Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse. [2] Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa, Mulungu wanga amene ndimadalira.” [3] Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje ndi ku mliri woopsa; [4] Adzakuphimba ndi nthenga zake, ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo; kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo. [5] Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku, kapena muvi wowuluka masana, [6] kapena mliri umene umayenda mu mdima, kapena zowononga za pa nthawi ya masana. [7] Anthu 1,000 atha kufa pambali pako, anthu 10,000 kudzanja lako lamanja, koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe. [8] Udzapenya ndi maso ako ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira. [9] Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo; wavomera Yehova kukhala kothawira kwako. [10] Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera, zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako. [11] Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse; [12] ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala. [13] Udzapondaponda mkango ndi njoka, udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka. [14] “Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa; ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa. [15] Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha; ndidzakhala naye pa mavuto, ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza. [16] Ndidzamupatsa moyo wautali ndi kumupulumutsa.”