Masalimo 90:1-17 OCCL

[1] Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo pa mibado yonse. [2] Mapiri asanabadwe, musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse, kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu. [3] Inu mumabwezera anthu ku fumbi, mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.” [4] Pakuti zaka 1,000 pamaso panu zili ngati tsiku limene lapita kapena ngati kamphindi ka usiku. [5] Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa, iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa, [6] ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano, pofika madzulo wauma ndi kufota. [7] Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu; ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu. [8] Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu, machimo athu obisika poonekera pamaso panu. [9] Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu; timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula. [10] Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70, kapena 80 ngati tili ndi mphamvu; komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa, zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali. [11] Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu? Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu. [12] Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola, kuti tikhale ndi mtima wanzeru. [13] Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Achitireni chifundo atumiki anu. [14] Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha, kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse. [15] Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa, kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto. [16] Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu, kukongola kwanu kwa ana awo. [17] Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife; tikhazikitsireni ntchito ya manja athu; inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.