Masalimo 92:1-15 OCCL

[1] Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba, [2] Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku, [3] kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze. [4] Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu. [5] Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi! [6] Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira, [7] kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya. [8] Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya. [9] Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa. [10] Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga. [11] Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa. [12] Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni; [13] odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu. [14] Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira, [15] kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.