[1] Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
[2] Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
[3] kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
[4] Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
[5] Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
[6] Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
[7] kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
[8] Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
[9] Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
[10] Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
[11] Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
[12] Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
[13] odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
[14] Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
[15] kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”