Masalimo 89:1-52 OCCL
[1] Ndidzayimba za chikondi chachikulu cha Yehova kwamuyaya; ndi pakamwa panga ndidzachititsa kuti kukhulupirika kwanu kudziwike ku mibado yonse. [2] Ndidzalalikira kuti chikondi chanu chidzakhazikika mpaka muyaya, kuti Inu munakhazikitsa kukhulupirika kwanu kumwamba kwenikweniko. [3] Inu munati, “Ndachita pangano ndi wosankhidwa wanga, ndalumbira kwa Davide mtumiki wanga kuti, [4] ‘Ndidzakhazikitsa zidzukulu zako mpaka muyaya. Ndidzachititsa kuti mpando wako waufumu ukhazikike ku mibado yonse,’ ” Sela. [5] Mayiko akumwamba amatamanda zozizwitsa zanu Yehova, kukhulupirika kwanunso, mu msonkhano wa oyera mtima anu. [6] Pakuti ndani mu mlengalenga angalingane ndi Yehova? Ndani wofanana ndi Yehova pakati pa zolengedwa zakumwamba? [7] Mu msonkhano wa oyera mtima Mulungu amaopedwa kwambiri; Iye ndiye wochititsa mantha kupambana onse amene amuzungulira. [8] Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndani wofanana nanu? Yehova ndinu wamphamvu ndipo kukhulupirika kwanu kwakuzungulirani. [9] Mumalamula nyanja ya mafunde awukali; pamene mafunde ake awundana Inu mumawakhalitsa bata. [10] Munaphwanya Rahabe monga munthu wophedwa; ndi dzanja lanu lamphamvu munabalalitsa adani anu. [11] Mayiko akumwamba ndi anu ndiponso dziko lapansi ndi lanu; munapanga dziko lonse ndi zonse zili mʼmenemo. [12] Munalenga Kumpoto ndi Kummwera; Tabori ndi Herimoni akuyimba ndi chimwemwe pa dzina lanu. [13] Mkono wanu ndi wamphamvu; dzanja lanu ndi lamphamvu, dzanja lanu lamanja ndi lopambana. [14] Chilungamo ndi chiweruzo cholungama ndiye maziko a mpando wanu waufumu; chikondi ndi kukhulupirika zimayenda patsogolo panu. [15] Ndi odala amene aphunzira kuyamika Inu, amene amayenda mʼkuwunika kwa nkhope yanu Yehova. [16] Amakondwera mʼdzina lanu tsiku lonse lathunthu; amasangalala koposa mʼchilungamo chanu. [17] Pakuti Inu ndiye ulemerero wawo ndi mphamvu yawo ndipo mwa kukoma mtima kwanu Inu mumakweza nyanga yathu. [18] Ndithudi, chishango chathu ndi cha Yehova, Mfumu yathu kwa Woyerayo wa Israeli. [19] Kale munayankhula mʼmasomphenya, kwa anthu anu okhulupirika munati, “Ndapatsa mphamvu wankhondo; ndakweza mnyamata wochokera pakati pa anthu. [20] Ndamupeza mtumiki wanga Davide; ndamudzoza ndi mafuta opatulika. [21] Dzanja langa lidzamuchirikiza; zoonadi, mkono wanga udzamupatsa mphamvu. [22] Adani sadzamulamula kuti apereke msonkho; anthu oyipa sadzamusautsa. [23] Ndidzaphwanya adani ake pamaso pake ndi kukantha otsutsana naye. [24] Chikondi changa chokhulupirika chidzakhala naye, ndipo kudzera mʼdzina langa nyanga yake idzakwezedwa. [25] Ndidzayika dzanja lake pa nyanja, dzanja lake lamanja pa mitsinje. [26] Iyeyo adzafuwula kwa Ine kuti, ‘Ndinu Atate anga, Mulungu wanga, Thanthwe ndi Chipulumutso changa.’ [27] Ndidzamuyika kuti akhale mwana wanga woyamba kubadwa; wokwezedwa kwambiri pakati pa mafumu a dziko lapansi. [28] Ndidzamusungira chifundo changa kwamuyaya, ndipo pangano langa ndi iye silidzatha. [29] Ine ndidzakhazikitsa zidzukulu zake mpaka muyaya, mpando wake waufumu ngati masiku a miyamba. [30] “Ngati ana ake adzataya lamulo langa ndi kusatsatira malangizo anga, [31] ngati adzaswa malamulo anga ndi kulephera kusunga ziphunzitso zanga, [32] Ine ndidzalanga tchimo lawo ndi ndodo, mphulupulu zawo powakwapula. [33] Koma sindidzachotsa chikondi changa pa iye, kapena kukhala wosakhulupirika kwa iyeyo. [34] Sindidzaswa pangano langa kapena kusintha zimene milomo yanga yayankhula. [35] Ndinalumbira kamodzi mwa kuyera kwanga ndipo sindidzanama kwa Davide, [36] kuti zidzukulu zake zidzakhale kwamuyaya ndipo mpando wake waufumu udzakhazikika pamaso panga ngati dzuwa; [37] udzakhazikika kwamuyaya monga mwezi, mboni yokhulupirika mʼmitambo. Sela [38] “Koma tsopano Inu mwamukana, mwamutaya, mwamukwiyira kwambiri wodzozedwa wanu. [39] Mwakana pangano ndi mtumiki wanu ndipo mwadetsa mʼfumbi chipewa chake chaufumu. [40] Inu mwagumula makoma ake onse ndipo mwasandutsa bwinja malinga ake. [41] Onse amene amadutsa amalanda zinthu zake; iye wakhala chotonzedwa cha anansi ake. [42] Mwakweza dzanja lamanja la adani ake; mwachititsa kuti adani ake akondwere. [43] Mwabunthitsa lupanga lake, simunamuthandize pa nkhondo. [44] Inu mwathetsa kukongola kwa ulemerero wake ndipo mwagwetsa pansi mpando wake waufumu. [45] Mwachepetsa masiku a unyamata wake; mwamuphimba ndi chofunda chochititsa manyazi. Sela [46] “Mpaka liti Yehova? Kodi mudzadzibisa mpaka kalekale? Mpaka liti ukali wanu udzayaka ngati moto? [47] Kumbukirani kuti masiku a moyo wanga ndi ochepa pakuti munalenga kwachabe anthu onse! [48] Kodi ndi munthu uti angakhale ndi moyo ndi kusaona imfa? Kapena kudzipulumutsa yekha ku mphamvu ya manda? Sela [49] Inu Ambuye kodi chili kuti chikondi chanu chachikulu choyamba chija, chimene mwa kukhulupirika kwanu munalumbira kwa Davide? [50] Kumbukirani, Ambuye momwe mtumiki wanu wanyozedwera, momwe ndakhalira ndi kusunga mu mtima mwanga mawu a pangano a anthu a mitundu yonse, [51] mawu achipongwe amene adani anu akhala akunyoza, Inu Yehova, ndi mawu amene akhala akunyoza mayendedwe onse a wodzozedwa wanu. [52] “Matamando akhale kwa Yehova mpaka muyaya!” Ameni ndi Ameni.
