Masalimo 88:1-18 OCCL

[1] Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu. [2] Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga. [3] Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. [4] Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu. [5] Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu. [6] Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu. [7] Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. Sela [8] Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa; [9] maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu. [10] Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? Sela [11] Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko? [12] Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika? [13] Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu. [14] Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu? [15] Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru. [16] Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga. [17] Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu. [18] Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.