[1] Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
[2] Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
[3] Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda.
[4] Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
[5] Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
[6] Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
[7] Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. Sela
[8] Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
[9] maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
[10] Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? Sela
[11] Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
[12] Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
[13] Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
[14] Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
[15] Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
[16] Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
[17] Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
[18] Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.