Masalimo 87:1-7 OCCL

[1] Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera; [2] Yehova amakonda zipata za Ziyoni kupambana malo onse okhalamo a Yakobo. [3] Za ulemerero wako zimakambidwa, Iwe mzinda wa Mulungu: Sela [4] “Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni pakati pa iwo amene amandidziwa. Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi, ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’ ” [5] Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti, “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye, ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.” [6] Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina: “Uyu anabadwira mʼZiyoni.” Sela [7] Oyimba ndi ovina omwe adzati, “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.