[1] Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
[2] Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
[3] Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
[4] Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
[5] Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
[6] Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
[7] Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
[8] Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
[9] Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
[10] Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
[11] Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
[12] Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
[13] asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
[14] Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
[15] Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
[16] nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
[17] Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
[18] Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
[19] Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
[20] Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
[21] Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
[22] Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.