[1] Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo. [2] Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi. [3] Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe. [4] Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita. [5] Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha. [6] Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake. [7] Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo. [8] Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye. [9] Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika. [10] Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri. [11] Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse. [12] Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake. [13] Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse; [14] kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi. [15] Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita. [16] Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu. [17] Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa. [18] Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha, [19] kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala. [20] Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu. [21] Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera. [22] Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.