Masalimo 35:1-28 OCCL
[1] Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane; mumenyane nawo amene akumenyana nane. [2] Tengani chishango ndi lihawo; dzukani ndipo bwerani mundithandize. [3] Tengani mkondo ndi nthungo, kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa. Uzani moyo wanga kuti, “Ine ndine chipulumutso chako.” [4] Iwo amene akufunafuna moyo wanga anyozedwe ndi kuchita manyazi; iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha. [5] Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa. [6] Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa. [7] Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje, [8] chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa ukonde umene iwo abisa uwakole, agwere mʼdzenje kuti awonongedwe. [9] Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova ndi kusangalala ndi chipulumutso chake. [10] Thupi langa lidzafuwula mokondwera, “Ndani angafanane nanu Yehova? Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri, osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.” [11] Mboni zopanda chisoni zinayimirira, zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa. [12] Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni. [13] Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya. Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa, [14] ndinayendayenda ndi kulira maliro, kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga. Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima kukhala ngati ndikulira amayi anga. [15] Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala; ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa. Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza. [16] Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe; anandikukutira mano awo. [17] Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana? Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo, moyo wanga wopambana ku mikango. [18] Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu; pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani. [19] Musalole adani anga onyenga akondwere chifukwa cha masautso anga; musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza. [20] Iwowo sayankhula mwamtendere, koma amaganizira zonamizira iwo amene amakhala mwabata mʼdziko. [21] Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa! Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.” [22] Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete. Ambuye musakhale kutali ndi ine. [23] Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza! Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga. [24] Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga. Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga. [25] Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!” Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.” [26] Onse amene amakondwera ndi masautso anga achite manyazi ndi kusokonezeka. Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana, avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala. [27] Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa, afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo. Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke, Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.” [28] Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu ndi za matamando anu tsiku lonse.
