Masalimo 149:1-9 OCCL

[1] Tamandani Yehova. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, matamando ake mu msonkhano wa oyera mtima. [2] Israeli asangalale mwa mlengi wake; anthu a ku Ziyoni akondwere mwa Mfumu yawo. [3] Atamande dzina lake povina ndi kuyimbira Iye nyimbo ndi tambolini ndi pangwe. [4] Pakuti Yehova amakondwera ndi anthu ake; Iye amaveka chipulumutso odzichepetsa. [5] Oyera mtima asangalale mu ulemu wake ndi kuyimba mwachimwemwe pa mabedi awo. [6] Matamando a Mulungu akhale pakamwa pawo, ndi lupanga lakuthwa konsekonse mʼmanja mwawo, [7] kubwezera chilango anthu a mitundu ina, ndi kulanga anthu a mitundu yonse, [8] kumanga mafumu awo ndi zingwe, anthu awo otchuka ndi unyolo wachitsulo, [9] kuchita zimene zinalembedwa zotsutsana nawo Uwu ndi ulemerero wa oyera mtima ake onse. Tamandani Yehova.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.