Masalimo 148:1-14 OCCL

[1] Tamandani Yehova. Tamandani Yehova, inu a kumwamba, mutamandeni Iye, inu a mlengalenga. [2] Mutamandeni, inu angelo ake onse, mutamandeni, mutamandeni, inu zolengedwa za mmwamba. [3] Mutamandeni, inu dzuwa ndi mwezi, mutamandeni, inu nonse nyenyezi zowala. [4] Mutamandeni, inu thambo la kumwambamwamba ndi inu madzi a pamwamba pa thambo. [5] Zonse zitamande dzina la Yehova pakuti Iye analamula ndipo zinalengedwa. [6] Iye anaziyika pa malo ake ku nthawi za nthawi; analamula ndipo sizidzatha. [7] Tamandani Yehova pa dziko lapansi, inu zolengedwa zikuluzikulu za mʼnyanja, ndi nyanja zonse zakuya, [8] inu zingʼaningʼani ndi matalala, chipale ndi mitambo, mphepo yamkuntho imene imakwaniritsa mawu ake, [9] inu mapiri ndi zitunda zonse, inu mitengo ya zipatso ndi mikungudza yonse, [10] inu nyama zakuthengo ndi ngʼombe zonse, inu zolengedwa zingʼonozingʼono ndi mbalame zowuluka. [11] Inu mafumu a dziko lapansi ndi anthu a mitundu yonse, inu akalonga ndi olamulira a dziko lapansi. [12] Inu anyamata ndi anamwali, inu nkhalamba ndi ana omwe. [13] Onsewo atamande dzina la Yehova pakuti dzina lake lokha ndi lolemekezeka; ulemerero wake ndi woopsa pa dziko lapansi pano ndi kumwamba komwe. [14] Iye wakwezera nyanga anthu ake, matamando a anthu ake onse oyera mtima, Aisraeli, anthu a pamtima pake. Tamandani Yehova.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.