[1] Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda! [2] Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli. [3] Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo. [4] Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina. [5] Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire. [6] Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa. [7] Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe. [8] Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri. [9] Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya. [10] Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu. [11] Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika. [12] Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni, [13] pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe. [14] Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala. [15] Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro. [16] Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa. [17] Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake? [18] Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda. [19] Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli. [20] Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.