[1] Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino. Pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [2] Yamikani Mulungu wa milungu. Pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [3] Yamikani Ambuye wa ambuye, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [4] Iye yekhayo amene amachita zodabwitsa zazikulu, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [5] Amene mwachidziwitso chake anapanga mayiko akumwamba, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [6] Amene anayala dziko lapansi pamwamba pa madzi, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [7] Amene anapanga miyuni ikuluikulu, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [8] Dzuwa lilamulire usana, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [9] Mwezi ndi nyenyezi zilamulire usiku, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [10] Amene anakantha ana woyamba kubadwa a Igupto, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [11] Natulutsa Israeli pakati pawo, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [12] Ndi dzanja lamphamvu ndi mkono wotambasuka, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [13] Amene anagawa Nyanja Yofiira pakati, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [14] Nadutsitsa Israeli pakati pa nyanjayo, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [15] Koma anakokolola Farao ndi ankhondo ake mʼNyanja Yofiira, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [16] Amene anatsogolera anthu ake mʼchipululu pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [17] Amene anakantha mafumu akuluakulu, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [18] Napha mafumu amphamvu, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [19] Siloni mfumu ya Aamori, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [20] Ogi mfumu ya Basani, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [21] Napereka dziko lawo ngati cholowa, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [22] Cholowa cha mtumiki wake Israeli; pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [23] Amene anatikumbukira ife anthu opeputsidwa, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [24] Amene anatimasula kwa adani athu, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [25] Amene amapereka chakudya kwa cholengedwa chilichonse, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya. [26] Yamikani Mulungu wakumwamba, pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.