[1] Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova, [2] amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu. [3] Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero, [4] Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima. [5] Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse. [6] Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya. [7] Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo. [8] Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama. [9] Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse. [10] Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu: [11] Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani; [12] ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli. [13] Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse. [14] Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake. [15] Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu. [16] Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya; [17] makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse. [18] Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo. [19] Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova; [20] Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova. [21] Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.