Masalimo 137:1-9 OCCL

[1] Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni. [2] Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu, [3] pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!” [4] Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo? [5] Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake. [6] Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu. [7] Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!” [8] Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira. [9] Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.