[1] Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni. [2] Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu, [3] pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!” [4] Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo? [5] Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake. [6] Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu. [7] Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!” [8] Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira. [9] Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.