Masalimo 129:1-8 OCCL

[1] “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli; [2] “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane. [3] Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali: [4] Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.” [5] Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi. [6] Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule; [7] sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo. [8] Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.