[1] Ndikulirira kwa Inu Yehova ndili mʼdzenje lozama;
[2] Ambuye imvani mawu anga. Makutu anu akhale tcheru kumva kupempha chifundo kwanga.
[3] Inu Yehova, mukanamawerengera machimo, Inu Yehova, akanayima chilili ndani wopanda mlandu?
[4] Koma kwa Inu kuli chikhululukiro; nʼchifukwa chake mumaopedwa.
[5] Ndimayembekezera Yehova, moyo wanga umayembekezera, ndipo ndimakhulupirira mawu ake.
[6] Moyo wanga umayembekezera Ambuye, kupambana momwe alonda amayembekezera mmawa, inde, kupambana momwe alonda amayembekezera mmawa,
[7] Yembekeza Yehova, iwe Israeli, pakuti Yehova ali ndi chikondi chosasinthika ndipo alinso ndi chipulumutso chochuluka.
[8] Iye mwini adzawombola Israeli ku machimo ake onse.