[1] Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
[2] Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
[3] Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
[4] Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
[5] Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
[6] ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.