Masalimo 127:1-5 OCCL

[1] Yehova akapanda kumanga nyumba, omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe. Yehova akapanda kulondera mzinda, mlonda akanangolondera pachabe. [2] Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa ndi kusagona msanga madzulo, kuvutikira chakudya choti mudye, pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda. [3] Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova, ana ndi mphotho yochokera kwa Iye. [4] Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja mwa munthu wankhondo. [5] Wodala munthu amene motengera mivi mwake mwadzaza. Iwo sadzachititsidwa manyazi pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.