[1] Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
[2] Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
[3] Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
[4] Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
[5] Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
[6] Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.