Masalimo 126:1-6 OCCL

[1] Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota. [2] Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.” [3] Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe. [4] Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi. [5] Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe. [6] Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.