[1] Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
[2] Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
[3] Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
[4] Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
[5] Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
[6] Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
[7] Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
[8] Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.