Masalimo 121:1-8 OCCL

[1] Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti? [2] Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi. [3] Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera. [4] Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona. [5] Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja. [6] Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku. [7] Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako. [8] Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.