Masalimo 122:1-9 OCCL

[1] Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.” [2] Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu. [3] Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi. [4] Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova. [5] Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide. [6] Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino. [7] Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.” [8] Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.” [9] Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.