[1] Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
[2] Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
[3] Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
[4] Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
[5] Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
[6] Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
[7] Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
[8] Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
[9] Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.