Masalimo 122:1-9 OCCL

[1] Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.” [2] Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu. [3] Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi. [4] Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova. [5] Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide. [6] Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino. [7] Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.” [8] Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.” [9] Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.