Masalimo 120:1-7 OCCL

[1] Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha. [2] Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo. [3] Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo? [4] Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya. [5] Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara! [6] Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere. [7] Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.