Masalimo 120:1-7 OCCL

[1] Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha. [2] Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo. [3] Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo? [4] Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya. [5] Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara! [6] Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere. [7] Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.