Masalimo 119:1-176 OCCL
[1] Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova. [2] Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse. [3] Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake. [4] Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu. [5] Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu! [6] Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse. [7] Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama. [8] Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu. [9] Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu. [10] Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu. [11] Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni. [12] Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu. [13] Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu. [14] Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri. [15] Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu. [16] Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu. [17] Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu. [18] Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu. [19] Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu. [20] Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse. [21] Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu. [22] Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu. [23] Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu. [24] Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza. [25] Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu. [26] Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu. [27] Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu. [28] Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu. [29] Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu. [30] Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga. [31] Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi. [32] Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga. [33] Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto. [34] Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse. [35] Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa. [36] Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma. [37] Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu. [38] Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe. [39] Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino. [40] Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu. [41] Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu; [42] ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu. [43] Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu. [44] Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi. [45] Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu. [46] Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi, [47] popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda. [48] Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu. [49] Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo. [50] Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga. [51] Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu. [52] Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo. [53] Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu. [54] Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako. [55] Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu. [56] Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu. [57] Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu. [58] Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu. [59] Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu. [60] Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu. [61] Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu. [62] Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama. [63] Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu. [64] Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu. [65] Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu. [66] Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu. [67] Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu. [68] Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu. [69] Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse. [70] Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu. [71] Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu. [72] Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide. [73] Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu. [74] Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu. [75] Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu. [76] Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu. [77] Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa. [78] Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu. [79] Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu. [80] Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi. [81] Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu. [82] Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?” [83] Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu. [84] Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza? [85] Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu. [86] Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa. [87] Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu. [88] Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu. [89] Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako. [90] Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe. [91] Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu. [92] Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga. [93] Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga. [94] Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu. [95] Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu. [96] Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse. [97] Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse. [98] Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse. [99] Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu. [100] Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu. [101] Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu. [102] Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa. [103] Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga! [104] Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa. [105] Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga. [106] Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama. [107] Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu. [108] Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu. [109] Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu. [110] Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu. [111] Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga. [112] Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni. [113] Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu. [114] Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu. [115] Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga! [116] Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe. [117] Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu. [118] Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu. [119] Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu. [120] Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu. [121] Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza. [122] Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze. [123] Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama. [124] Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu. [125] Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu. [126] Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa. [127] Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino, [128] ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa. [129] Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera. [130] Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa. [131] Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu. [132] Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu. [133] Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira. [134] Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu. [135] Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu. [136] Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu. [137] Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino. [138] Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu. [139] Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu. [140] Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda. [141] Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu. [142] Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona. [143] Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu. [144] Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo. [145] Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu. [146] Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu. [147] Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu. [148] Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu. [149] Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu. [150] Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu. [151] Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona. [152] Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya. [153] Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu. [154] Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu. [155] Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu. [156] Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu. [157] Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu. [158] Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu. [159] Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika. [160] Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya. [161] Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu. [162] Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri. [163] Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu. [164] Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama. [165] Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse [166] Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu. [167] Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri. [168] Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu. [169] Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu. [170] Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu. [171] Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu. [172] Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama. [173] Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu. [174] Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu. [175] Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize. [176] Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
