Masalimo 118:1-29 OCCL
[1] Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha. [2] Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.” [3] Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.” [4] Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.” [5] Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo. [6] Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani? [7] Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano. [8] Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu. [9] Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu. [10] Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga. [11] Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga. [12] Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga. [13] Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza. [14] Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa. [15] Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu! [16] Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!” [17] Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova. [18] Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa. [19] Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova. [20] Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo. [21] Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa. [22] Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya; [23] Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu. [24] Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo. [25] Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni. [26] Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova. [27] Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa. [28] Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani. [29] Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
