[1] Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu. [2] Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?” [3] Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa. [4] Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu. [5] Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya; [6] makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza; [7] manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu. [8] Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo. [9] Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu. [10] Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako. [11] Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu. [12] Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni, [13] adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe. [14] Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu. [15] Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi. [16] Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu. [17] Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete; [18] ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.