[1] Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo. [2] Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga. [3] Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. [4] Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!” [5] Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo. [6] Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa. [7] Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma. [8] Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe, [9] kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo. [10] Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.” [11] Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.” [12] Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira? [13] Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova. [14] Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse. [15] Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova. [16] Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga. [17] Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova. [18] Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse, [19] mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.