Masalimo 114:1-8 OCCL

[1] Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo, [2] Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake. [3] Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo; [4] mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa. [5] Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo? [6] inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa? [7] Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo, [8] amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.