Masalimo 113:1-9 OCCL

[1] Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova. [2] Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya. [3] Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa. [4] Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba. [5] Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba? [6] amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi? [7] Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala; [8] amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake. [9] Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.

About this translation

Life Bible app icon
Get the Life Bible app ★★★★★4.8 · 216K ratings Read offline, sync highlights and notes, and study with your library on any device.