Masalimo 106:1-48 OCCL
[1] Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha. [2] Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira? [3] Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse. [4] Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo, [5] kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani. [6] Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa. [7] Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira. [8] Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu. [9] Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu. [10] Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani. [11] Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka. [12] Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando. [13] Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake. [14] Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu. [15] Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa. [16] Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira. [17] Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu. [18] Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa. [19] Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo. [20] Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu. [21] Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto, [22] zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira. [23] Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge. [24] Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake. [25] Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova. [26] Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu, [27] kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse. [28] Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo; [29] anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo. [30] Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka. [31] Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera. [32] Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo, [33] pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera. [34] Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira. [35] Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo. [36] Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo. [37] Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda. [38] Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo. [39] Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo. [40] Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake. [41] Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira. [42] Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo. [43] Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo. [44] Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo; [45] Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake. [46] Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni. [47] Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu. [48] Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.
